Рет қаралды 27,105
MMENE JOE GWALADI ANAPANGIRA MA MILLION AKE
Woyimba wapakanthawi Joe Gwaladi ndi mmdzi mwa oyimba womwe ali ndi luso lakutha kupeka nyimbo mwaukadaulo ndipo zomwe amayimba zimadzafanana ndi zomwe anthu pa moyo akukumana nazo. Munanverako nyimbo yotchedwa Chipepeso yomwe amapempha aliyense kuti amupatsiretu chipepeso chake asanamwalire kuti mwina angodyeratu kuwopa kudzapereka atamwalira abale ake mkudzamakanganirana? Nanga ngati simunaimnvere, Tumbocid bwa? Iyi ndi nyimbo yomwe imapempha anthu kuti asalimbane ndi kumwa mankhwala osiyanasiyana akamva kuwawa kwa mthupi ndipo angopita ku chipatala kuti akayesetse magazi awo. Pa nthawi yomwe inatuluka nyimbo mu chaka cha 2012, inafika paliponse mdziko muno ndipo anthu ambiri anayamba kumafalitsa kuti Joe Gwaladi watola chikwama popeza aku unduna wa za umoyo ndi omwe anamutuma kuti ayimbe ndipo amulipira ndalama zambiri.